24. Wa ana a Uziyeli, Mika; wa ana a Mika, Samiri.
25. Mbale wa Mika, Isiya; a ana a Isiya, Zekariya,
26. Ana a Merari: Mali ndi Musi; mwana wa Yaziya, Beno.
27. Ana a Merari: wa Yaziya, Beno, ndi Sohamu, ndi Sakuri, ndi Ibri.
28. Wa Mali: Eleazara, ndiye wopanda ana.
29. Wa Kisi: mwana wa Kisi, Yerameli.
30. Ndi ana a Musi: Mali, ndi Ederi, ndi Yerimoti, Awa ndi ana a Alevi monga mwa nyumba za makolo ao.
31. Awanso anacita maere monga abale ao ana a Aroni, pamaso pa Davide mfumu, ndi Zadoki, ndi Ahimeleki, ndi akuru a nyumba za makolo za ansembe ndi Alevi; mkuru wa nyumba za makolo monga mng'ono wace.