Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 2:20-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndi Huri anabala Uri, ndi Uri anabala Bezaleli.

21. Ndipo pambuyo pace Hezroni analowa kwa mwana wamkazi wa Makiri atate wa Gileadi, amene anamtenga akhale mkazi wace, pokhala wa zaka makumi asanu ndi Gmodzi mwamunayo; ndipo mkaziyo anambalira Segubu.

22. Ndi Segubu anabala Yairi, amene anali nayo midzi makumi awiri mphambu itatu m'dziko la Gileadi.

23. Ndi Gesuri ndi Aramu analanda midzi ya Yairi, pamodzi ndi Kenati ndi miraga yace; ndiyo midzi makumi asanu ndi limodzi. Iwo onse ndiwo ana a Makiri atate wa Gileadi.

24. Ndipo atafa Hezroni m'Kalebi-Efrata, Abiya mkazi wa Hezroni anambalira Asini atate wa Tekoa.

25. Ndi ana a Yerameli mwana woyamba wa Hezroni ndiwo: woyamba Ramu, ndi Buna, ndi Oreni, ndi Ozemu, ndi Ahiya.

26. Ndipo Yerameli anali naye mkazi wina dzina lace ndiye Atara, ndiye mace wa Onamu.

27. Ndipo ana a Ramu mwana woyamba wa Yerameli ndiwo Maazi, ndi Yamini, ndi Ekeri.

28. Ndi ana a Onamu ndiwo Samai, ndi Yada; ndi ana a Samai: Nadabu, ndi Abisuri.

29. Ndipo dzina la mkazi wa Abisuri ndiye Abihaili; ndipo anambalira Abani, ndi Molidi.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 2