13. ndi Jese anabala mwana wace wamwamuna woyamba Eliabu, ndi Abinadabu waciwiri, ndi Simeya wacitatu,
14. Netaneli wacinai, Radai wacisanu,
15. Ozemu wacisanu ndi cimodzi, Davide wacisanu ndi ciwiri;
16. ndi alongo ao ndiwo Zeruya ndi Abigaili. Ndi ana a Zeruya: Abisai ndi Yoabu, ndi Asaheli; atatu.
17. Ndi Abigaili anabala Amasa; ndi atate wa Amasa ndiye Yeteri M-ismayeli.
18. Ndi Kalebi mwana wa Hezroni anabala ana ndi Azuba mkazi wace, ndi Yerioti; ndipo ana ace ndiwo Yeseri, ndi Sobabu, ndi Aridoni.
19. Namwalira Azuba, ndi Kalebi anadzitengera Efrati, amene anambalira Huri.