Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 12:36-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Ndi a Aseri akuturuka kukhamu, akupangira nkhondo, zikwi makumi anai.

37. Ndi tsidya lga la Yordano a Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la: Manase logawika pakati, ndi zida: ziri zonse za khamu kucita nazo nkhondo, zikwi zana limodzi ndi makumi awiri.

38. Onsewa, ndiwo anthu a nkhondo akusunga malongosoledwe a nkhondo, anadza ku Hebroni ndi mtima wangwiro kudzamlonga Davide mfumu ya Aisraeli onse; ndi onse otsala a Israyeli omwe anali a mtima umodzi kumlonga Davide ufumu.

39. Ndipo anali komweko kwa Davide masiku atatu kudya ndi kumwa, popeza abale ao-anazikonzeratu.

40. Ndiponso akuyandikizana nao mpaka Isakara ndi Zebuloni ndi Nafitali anabwera nao mkate osenzetsa aburu, ndi ngamira, ndi nyuru, ndi ng'ombe, zakudya zaufa, ndi ncinci zankhuyu, ndi ncinci zamphesa, ndi vinyo, ndi mafuta, ndi ng'ombe, ndi nkhosa zocuruka; pakuti munali cimwemwe m'Israyeli.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 12