26. A ana a Levi zikwi zinai mphambu mazana asanu ndi limodzi.
27. Ndipo Yehoyada, ndiye mtsogoleri wa Aaroni, ndi pamodzi nave zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi awiri;
28. ndi Zadoki, ndiye mnyamata, ngwazi yamphamvu, ndi a nyumba ya kholo lace, akuru makumi awiri mphambu awfri.
29. Ndi a ana a Benjamini, abale a Sauli, zikwi zitatu; pakuti mpaka pomwepo ocuruka a iwowa anaumirira nyumba ya Sauli.
30. Ndi a ana a Efraimu zikwi makumi awiri mphambu mazana asanu ndi atatu, ngwazi zamphamvu, anthu omveka m'nyumba za makolo ao.
31. Ndipo a pfuko la Manase logawika pakati zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu, ochulidwa maina ao kuti adzalonge Davide mfumu.
32. Ndi a ana a Isakara, anthu akuzindikira nyengo, akudziwa zoyenera Israyeli kuzicita, akuru ao ndiwo mazana awiri; ndi abale ao onse anapenyerera pakamwa pao.
33. A Zebuloni akuturuka kukhamu, opangira nkhondo, monga mwa zida ziri zonse za nkhondo, zikwi makumi asanu, akusunga malongosoledwe a nkhondo ndi mtima wosatekeseka.
34. Ndi a Nafitali atsogoleri cikwi cimodzi, ndi pamodzi nao ogwira zikopa ndi mikondo zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi ziwiri.
35. Ndi a Adani akupangira nkhondo zikwi makumi awiri mphambu zisanu ndi zitatu kudza mazana asanu ndi limodzi.
36. Ndi a Aseri akuturuka kukhamu, akupangira nkhondo, zikwi makumi anai.
37. Ndi tsidya lga la Yordano a Arubeni, ndi Agadi, ndi pfuko la: Manase logawika pakati, ndi zida: ziri zonse za khamu kucita nazo nkhondo, zikwi zana limodzi ndi makumi awiri.
38. Onsewa, ndiwo anthu a nkhondo akusunga malongosoledwe a nkhondo, anadza ku Hebroni ndi mtima wangwiro kudzamlonga Davide mfumu ya Aisraeli onse; ndi onse otsala a Israyeli omwe anali a mtima umodzi kumlonga Davide ufumu.
39. Ndipo anali komweko kwa Davide masiku atatu kudya ndi kumwa, popeza abale ao-anazikonzeratu.