Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mbiri 1:46-54 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. Namwalira Husamu; ndi Hadada mwana wa Bedadi, amene anakantha Midyani ku thengo la Moabu, anakhala mfumu m'malo mwace; ndi dzina la mudzi wace ndi Aviti.

47. Namwalira Hadada; ndi Samla wa ku Masereka anakhala mfumu m'malo mwace.

48. Namwalira Samla: ndi Sauli wa ku Rehoboti ku nyanja anakhala mfumu m'malo mwace.

49. Namwalira Sauli; ndi Baalahanani mwana wa Akiboro anakhala mfumu m'malo mwace.

50. Namwalira Baalahanani; ndi Hadada anakhala mfumu m'malo mwace; ndipo dzina la mudzi wace ndi Pai; ndi dzina la mkazi wace ndiye Mehetabele mwana wamkazi wa Matradi mwana wamkazi wa Mezahabu.

51. Namwalira Hadada. Ndipo mafumu a Edomu ndiwo mfumu Timna, mfumu Aliya, mfumu Yeteti;

52. mfumu Oholibama, mfumu Bla, mfumu Pimoni;

53. mfumu Kenazi, mfumu Temani, mfumu Mizibara;

54. mfumu Magadieli, mfumu Iramu. Awa ndi mafumu a Edomu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mbiri 1