Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 6:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo anakonza monenera m'kati mwa nyumba m'tsogolo mwace, kuikamo likasa la cipangano la Yehova.

20. Ndipo m'kati mwa monenera m'menemo, m'litali mwace munali mikono makumi awiri, kupingasa kwace mikono makumi awiri, ndi msinkhu wace mikono makumi awiri; ndipo anamukuta ndi golidi woyengetsa, nakutanso guwa la nsembe ndi matabwa amkungudza,

21. Momwemo Solomo anakuta m'kati mwa nyumba ndi golidi woyengetsa, natambalika maunyolo agolidi cakuno ca monenera, namukuta ndi golidi.

22. Ndipo nyumba yonse anaikuta ndi golidi mpaka adatha nyumba yonse, ndi guwa lonse la nsembe linali cakuno ca monenera analikuta ndi golidi.

23. Ndipo m'moneneramo anasema mitengo yaazitona akerubi awiri, yense wa msinkhu wace mikono khumi.

24. Ndipo phiko limodzi la kerubi linali la mikono isanu, ndi phiko lina la kerubi linalinso la mikono isanu; kuyambira ku nsonga ya phiko limodzi kufikira ku nsonga ya phiko lina inali mikono khumi.

25. Ndi kerubi winayo msinkhu wace unali mikono khumi; akerubi onse awiri anafanana muyeso wao ndi msinkhu wao.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 6