Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 4:14-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Abinadabu mwana wa Ido ku Nahanaimu;

15. Ahimazi ku Nafitali, iyeyu adakwatira Basemati mwana wa Solomo;

16. Baana mwana wa Husayi ku Aseri ndi ku Aloti;

17. Yehosafati mwana wa Paruwa ku Isakara;

18. Simeyi mwana wa Ela ku Benjamini;

19. Geberi mwana wa Uri ku dziko la Gileadi, dziko la Sihoni mfumu ya Aamori, ndi la Ogi mfumu ya Basani; munalibe kapitao wina m'deramo.

20. Ayuda ndi Aisrayeli anacuruka ngati mcenga wa kunyanja, namadya namamwa namakondwera.

21. Ndipo Solomo analamulira maiko onse, kuyambira ku Firate kufikira ku dziko la Afilisti ndi ku malire a Aigupto; anthu anabwera nayo mitulo namtumikira Solomo masiku onse a moyo wace.

22. Ndipo zakudya za Solomo zofikira tsiku limodzi zinalr miyeso makumi atatu ya ufa wosalala, ndi miyeso makumi asanu ndi limodzi ya ufa wamankhupete,

23. ng'ombe zonenepa khumi, ndi ng'ombe za kubusa makumi awiri, ndi nkhosa zana limodzi, osawerenganso ngondo ndi nswala ndi mphoyo ndi mbalame zoweta.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 4