Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 4:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Baana mwana wa Ahiludi ku Tanaki ndi Megido ndi Betseani konse, ali pafupi ndi Zaratana kunsi kwa Yezreeli, kuyambira ku Betseani kufikira ku Abelimehola, kufikiranso kundunji ku Yokineamu;

13. Benigeheri ku Ramoti Gileadi, iyeyo anali nayo midzi ya Yairo mwana wa Manase iri m'Gileadiyo, iye anali nalo dziko la Arigobi liri m'Basani, midzi yaikuru makumi asanu ndi limodzi yamalinga ndi zitseko zamkuwa;

14. Abinadabu mwana wa Ido ku Nahanaimu;

15. Ahimazi ku Nafitali, iyeyu adakwatira Basemati mwana wa Solomo;

16. Baana mwana wa Husayi ku Aseri ndi ku Aloti;

17. Yehosafati mwana wa Paruwa ku Isakara;

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 4