Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 22:46-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

46. Ndipo anacotsa m'dziko anyamata onyansa aja adatsalira masiku a atate wace Asa.

47. Ndipo m'Edomu munalibe mfumu, koma kazembe wa mfumu.

48. Yehosafati anamanga zombo za ku Tarsisi kukatenga golidi ku Ofiri; koma sizinamuka, popeza zinaphwanyika pa Ezioni Geberi.

49. Pamenepo Ahaziyamwana wa Ahabu ananena ndi Yehosafati, Anyamata anga amuke pamodzi ndi anyamata anu m'zombo. Koma Yehosafati anakana.

50. Ndipo Yehosafati anagona ndi makolo ace, naikidwa ndi makolo ace m'mudzi wa Davide kholo lace; ndipo Yoramu mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 22