4. Ndipo kudzakhala kuti uzikamwa mumtsinje, ndipo ndalamulira makungubwi kukudyetsa kumeneko.
5. Momwemo iye anamuka, nacita monga mwa mau a Yehova, nakakhala kumtsinje Keriti uli ku Yordano.
6. Ndipo makungubwi anamtengera mkate ndi nyama m'mawa, ndi mkate ndi nyama madzulo; namamwa iye mumtsinje.
7. Ndipo kunacitika, atapita masiku ena mtsinje udaphwa, popeza munalibe mvula m'dziko.
8. Ndipo mau a Yehova anadza kwa iye, nati,