Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 17:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo kudzakhala kuti uzikamwa mumtsinje, ndipo ndalamulira makungubwi kukudyetsa kumeneko.

5. Momwemo iye anamuka, nacita monga mwa mau a Yehova, nakakhala kumtsinje Keriti uli ku Yordano.

6. Ndipo makungubwi anamtengera mkate ndi nyama m'mawa, ndi mkate ndi nyama madzulo; namamwa iye mumtsinje.

7. Ndipo kunacitika, atapita masiku ena mtsinje udaphwa, popeza munalibe mvula m'dziko.

8. Ndipo mau a Yehova anadza kwa iye, nati,

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 17