Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 17:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Eliya wa ku Tisibe wokhala ku Gileadi ananena ndi Ahabu, nati, Pali Yehova Mulungu wa Israyeli, amene ndimakhala pamaso pace, ngati adzagwa mame kapena mvula zaka izi, koma ntanena ine ndipo.

2. Ndipo mau a Yehova anadza kwa iye, nati,

3. Coka kuno, nutembenukire kum'mawa, ukabisale kumtsinje Keriti uli ku Yordano.

4. Ndipo kudzakhala kuti uzikamwa mumtsinje, ndipo ndalamulira makungubwi kukudyetsa kumeneko.

5. Momwemo iye anamuka, nacita monga mwa mau a Yehova, nakakhala kumtsinje Keriti uli ku Yordano.

6. Ndipo makungubwi anamtengera mkate ndi nyama m'mawa, ndi mkate ndi nyama madzulo; namamwa iye mumtsinje.

7. Ndipo kunacitika, atapita masiku ena mtsinje udaphwa, popeza munalibe mvula m'dziko.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 17