Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 14:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo Aisrayeli onse adzamlira, nadzamuika, popeza iye yekha wa ana a Yerobiamu adzalowa m'manda; pakuti mwa iye mwapezedwa cokoma ca kwa Yehova Mulungu wa Israyeli m'nyumba ya Yerobiamu.

14. Ndiponso Yehova adzadziukitsira mfumu ya Israyeli, idzaononga nyumba ya Yerobiamu tsiku lomwelo; nciani ngakhale tsopano apa?

15. Popeza Yehova adzawakantha Aisrayeli monga bango ligwedezeka ndi madzi, nadzazula Aisrayeli m'dziko lino labwino analipatsa makolo ao, nadzawamwazira ku tsidya lija la Firate, popeza iwo anapanga zifanizo zao zokwiyitsa Yehova.

16. Ndipo adzai pereka Aisrayeli cifukwa ca macimo a Yerobiamu anacimwawo, nacimwitsa nao Aisrayeli.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 14