Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 13:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Tsono anabwerera naye, nakadya kwao, namwa madzi.

20. Ndipo kunacitika iwo ali cikhalire pagome, mau a Yehova anadza kwa mneneri amene anambwezayo,

21. napfuula iye kwa munthu uja wa Mulungu anacokera ku Yudayo, nati, Atero Yehova, Pokhala sunamvera mau a pakamwa pa Yehova, osasunga lamulo lija Yehova Mulungu wako anakulamulira,

22. koma unabwerera nudya mkate, ndi kumwa madzi paja pomwe iye anakuuza, Usakadye mkate, kapena kumwa madzi, mtembo wako tsono sudzaikidwa ku manda a atate ako.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 13