Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 12:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Rehabiamu anamka ku Sekemu, popeza Aisrayeli onse anadza ku Sekemu kumlonga ufumu.

2. Ndipo kunali kuti Yerobiamu mwana wa Nebati anacimva akali m'Aigupto, kumene anathawira kucokera ku maso a Solomo mfumu, pakuti Yerobiamu anakhala ku Aigupto.

3. Ndipo anatuma akukamuitana. Ndipo Yerobiamu ndi msonkhano wonse wa Israyeli anadza, nalankhulana ndi Rehabiamu, nati,

4. Atate wa nu analemeretsa gori lathu, ndipo inu tsono pepuzaniko nchito zosautsa za atate wanu, ndi gori lolemera lace limene anatisenza, ndipo tidzakutumikirani.

5. Ndipo iye anati kwa iwo, Bamukani, mukagone masiku atatu, pamenepo mukabwera kwa ine. Ndipo anthu anamuka.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 12