6. Koma inu mumanyoza munthu wosauka. Kodi sakusautsani inu acuma, nakukokerani iwowa ku mabwalo a mirandu?
7. Kodi sacitira mwano iwowa dzina lokomali muitanidwa nalo?
8. Koma ngati mucita cikwanirire lamulolo lacifumu, monga mwa malembo, Uzikonda mnzako monga udzikonda wekha, mucita bwino:
9. koma ngati musamala maonekedwe, mucita ucimo, ndipo mutsutsidwa ndi cilamulo monga olakwa.