32. Ndipo anthu ambiri anakhala pansi pomzinga; nanena kwa Iye, Onani, amanu ndi abale anu ali kunja akufunani Inu.
33. Ndipo anawayankha nanena, Amai wanga ndi abale anga ndani?
34. Ndipo anawaunguza-unguza iwo akumzingawo, nanena, Taonani, amai wanga ndi abale anga.
35. Pakuti ali yense acita cifuniro ca Mulungu, yemweyo ndiye mbale wanga, ndi mlongo, ndi amai.