15. Ndipo Pilato pofuna kuwakhazika mtima anthuwo, anawamasulira Baraba, napereka Yesu, atamkwapula, akampacike pamtanda.
16. Ndipo asilikari anacoka naye nalowa m'bwalo, ndilo Pretorio; nasonkhanitsa gulu lao lonse.
17. Ndipo anambveka Iye cibakuwa, naluka korona waminga, nambveka pa Iye;
18. ndipo anayamba kumlankhula Iye, kuti, Tikuoneni, Mfumu ya Ayuda!