34. Monga ngati munthu wa paulendo, adacoka kunyumba kwace, nawapatsa akapolo ace ulamuliro, kwa munthu ali yense nchito yace, nalamulira wapakhomo adikire.
35. Cifukwa cace dikirani; pakuti simudziwa inu nthawi yace yakubwera mwini nyumba, kapena madzulo, kapena pakati pausiku, kapena pakulira tambala, kapena mamawa;
36. kuti angabwere balamantha nakakupezani muli m'tulo.
37. Ndipo cimene ndinena ndi inu ndinena kwa onse, Dikirani.