56. nati, Taonani, 26 ndipenya m'Mwamba motseguka, ndi Mwana wa munthu alikuimirira pa dzanja lamanja la Mulungu.
57. Koma anapfuula ndi mau akuru, natseka m'makutu mwao, namgumukira iye ndi mtima umodzi;
58. ndipo 27 anamtaya kunja kwa mudzi, namponya miyala; ndipo 28 mbonizo zinaika zobvala zao pa mapazi a mnyamata dzina lace Saulo.
59. Ndipo anamponya miyala Stefano, alikuitana Ambuye, ndi kunena, 29 Ambuye Yesu, landirani mzimu wanga.