27. koma iye wakumcitira mnzace coipa anamkankha, nati, Wakuika iwe ndani mkulu ndi wotiweruzira?
28. 1 Kodi ufuna kundipha ine, monga muja unapha M-aigupto dzulo?
29. 2 Ndipo Mose anathawa pa mau awa, nakhala mlendo m'dziko la Midyani; kumeneko anabala ana amuna awiri.
30. Ndipo 3 zitapita zaka makumi anai, anamuonekera mngelo m'cipululu ca Sina, m'lawi la mota wa m'citsamba.
31. 4 Koma Mose pakuona, anazizwa pa coonekaco; ndipo pakuyandikira iye kukaona, kunadza mau a Ambuye,
32. 5 akuti, Ine ndine Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, ndi wa Isake, ndi wa Yakobo. Ndipo Mose ananthunthumira, osalimbika mtima kupenyetsako.