30. nawaturutsira iwo kunja, nati, Ambuye, ndicitenji kuti ndipulumuke?
31. Ndipo iwo anati, Ukhulupirire Ambuye Yesu, ndipo udzapulumuka, iwe ndi apabanja ako.
32. Ndipo anamuuza iye mau a Ambuye, pamodzi ndi onse a pabanja pace.
33. Ndipo anawatenga ora lomwelo la usiku, natsuka mikwingwirima yao; nabatizidwa pomwepo, iye ndi a pabanja pace.
34. Ndipo anakwera nao kunka kunyumba kwace, nawakhazikira cakudya, nasangalala kwambiri, pamodzi ndi a pabanja pace, atakhulupirira Mulungu.
35. Kutaca, oweruza anatumiza akapitao, kuti, Mukamasule anthu aja.
36. Ndipo mdindo anafotokozera mauwo kwa Paulo, nati, Oweruza atumiza mau kunena kuti mumuke; tsopanotu turukani, mukani mumtendere.
37. Koma Paulo anati kwa iwo, Adatikwapula ire pamaso pa anthu, osamva mlandu wathu, ire amene tiri Aroma, natiika m'ndende; ndipo tsopano kodi afuna kutiturutsira ire m'tseri? Iai, ndithu; koma adze okha atiturutse.
38. Ndipo akapitao anafotokozera mauwo kwa oweruza; ndipo iwowo anaopa, pakumva kuti anali Aroma.
39. Ndipo anadza nawapembedza; ndipo pamene anawaturutsa, anawapempha kuti acoke pamudzi.
40. Ndipo anaturukam'ndendemo, nalowa m'nyumba ya Lidiya: ndipo pamene anaona abale, anawasangalatsa, namuka.