27. Tatumiza tsono Yuda ndi Sila, omwenso adzakuuzani ndi mau zinthu zomwezo.
28. Pakuti cinakomer a Mzimu Woyera ndi ife, kuti tisasenzetse inu cothodwetsa cacikuru cina coposa izi zoyenerazi;
29. kuti musale nsembe za mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama; ngati mudzisungitsa pa zimenezi, kudzakhala bwino kwa inu. Tsalani bwino.
30. Tsono pamene iwo anamuka anatsikira ku Antiokeya; ndipo anasonkhanitsa khamu, napereka kalatayo.
31. Pamene anawerenga, anakondwera cifukwa ca cisangalatso cace.