15. Ndipo mau a aneneri abvomereza pamenepo; monga kunalembedwa,
16. Zikatha izo ndidzabwera, Ndidzamanganso cihema ca Davine, cimene cinagwa;Ndidzamanganso zopasuka zace,Ndipo ndidzaciimikanso:
17. Kuti anthu otsalira afunefune Ambuye,Ndi amitundu onse amene dzina langa linachulidwa pa iwo,
18. Ati Ambuye, amene azidziwitsa zinthu zonsezo ciyambire dzikolapansi.
19. Cifukwa cace ine ndiweruza, kuti tisabvute a mwa amitundu amene anatembenukira kwa Mulungu,
20. koma kuti tilembere kwa iwo, kuti asale zonyansa za mafano, ndi dama, ndi zopotola, ndi mwazi.