1. Pamene Yesu adamariza mau ace onse m'makutu a anthu, analowa m'Kapernao.
2. Ndipo kapolo wa kenturiyo, wokondedwa naye, anadwala, nafuna kutsirizika.
3. Ndipo pamene iye ana-I mva za Yesu, anatuma kwa iye akuru a Ayuda, namfunsa iye kuti adze kupulumutsa kapolo wace.
4. Ndipo iwo, pakufika kwa Yesu, anampempha iye koumirira, nati, Ayenera iye kuti mumcitire ici;
5. pakuti akonda mtundu wathu, ndipo anatimangira ife sunagoge.
6. Ndipo Yesu anapita nao. Ndipo pakufika iye tsono pafupi panyumba yace, kenturiyo anatuma kwa iye abwenzi ace, kunena naye, Ambuye, musadzibvute; pakuti sindiyenera ine kuti mudzalowe pansi pa chindwi langa;