36. Ndipo pakulankhula izi iwowa, iye anaimirira pakati pao; nanena nao, Mtendere ukhale nanu.
37. Koma anaopsedwandi kucita mantha, 1 nayesa alikuona mzimu.
38. Ndipo anati kwa iwo, Mukhala bwanji obvutika? ndipo matsutsano am auka bwanji m'mtima mwanu?
39. Penyani manja anga ndi mapazianga, kuti Ine ndine mwini: 2 ndikhudzeni, ndipo penyani; pakuti mzimu ulibe, mnofu ndi mafupa, monga muona ndirinazo Ine.
40. Ndipo m'mene ananena ici, anawaonetsera iwo manja ace ndi mapazi ace.