19. ndiye munthu anaponyedwa m'ndende cifukwa ca mpanduko m'mudzi ndi ca kupha munthu.
20. Ndipo Pilato analankhulanso nao, nafuna kumasula Yesu;
21. koma iwo anapfuula, nanena, Mpacikeni, mpacikeni pamtanda.
22. Ndipo anati kwa iwo nthawi yacitatu, Nanga munthuyu anacita coipa ciani? Sindinapeza cifukwa ca kufera iye; cotero ndidzamkwapula iye ndi kummasula.
23. Koma anakakamiza ndi mau okweza, napempha kuti iye apacikidwe, Ndipo mau ao analakika.
24. Ndipo Pilato anaweruza kuti cimene alikufunsa cicitidwe.