3. Ndipo m'mudzimo munali mkazi wamasiye; ndipo anadza kwa iye nanena, Mundiweruzire mlandu pa wotsutsana nane.
4. Ndipo sanafuna nthawi; koma bwino bwino anati mwa yekha, Ndingakhale sindiopa Mulungu kapena kusamala munthu;
5. koma cifukwa ca kundibvuta ine mkazi wamasiye amene ndidzamweruzira mlandu, kuti angandilemetse ndi kudzaidza kwace.
6. Ndipo Ambuye anati, Tamverani conena woweruza wosalungama.