22. Koma undikonzerenso pogona; pakuti ndiyembekeza kuti mwa mapemphero anu ndidzapatsidwa kwa inu.
23. Epafra wandende mnzanga mwa Kristu Yesu akulankhula iwe;
24. ateronso, Marko, Aristarko, Dema, Luka, anchito anzanga.
25. Cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu cikhale pamodzi ndi mzimu wanu. Amen.