17. Ngati tsono undiyesa woyanjana nawe, umlandire iye monga ine mwini.
18. Koma ngati anakulakwira kanthu, kapena wakongola kanthu, undiwerengere ine kameneko;
19. Ine Paulo ndicilemba ndi dzanja langa, ndidzacibwezera ine; kuti ndisanene nawe kuti iwe ndiwe mangawa anga.
20. Inde, mbale, ndikondwere nawe mwa Ambuye: utsitsimutse mtima wanga mwa Kristu.