22. Cifukwa cace ici cinawerengedwa kwa iye cilungamo.
23. Ndipo ici sicinalembedwa cifukwa caiye yekha yekha, kuti cidawerengedwa kwa iye;
24. koma cifukwa ca ifenso, kwa ife amene cidzawerengedwa kwa ife amene tikhulupirira iye amene anaukitsa kwa akufa Yesu Ambuye wathu,
25. amene anaperekedwa cifukwa ca zolakwazathu, naukitsidwa cifukwa ca kutiyesa ife olungama.