13. pakuti akumvaimva lamulo sakhala olungama pamaso pa Mulungu, koma akucita lamulo adzayesedwa olungama,
14. Pakuti pamene anthu a mitundu akukhala opanda lamulo, amacita mwa okha za lamulo, omwewo angakhale alibe lamulo, adzikhalira okha ngati lamulo;
15. popeza iwo aonetsa nchito ya lamulolo yolembedwa m'mitima yao, ndipo cikumbu mtima cao cicitiranso umboni pamodzi nao, ndipo maganizo ao wina ndi mnzace anenezana kapena akanirana;
16. tsiku limene Mulungu adzaweruza ndi Yesu Kristu zinsinsi za anthu, monga mwa uthenga wanga wabwino.
17. Koma ngati iwe unenedwa Myuda, nukhazikika palamulo, nudzitamandira pa Mulungu;
18. nudziwa cifuniro cace, nubvomereza zinthu zoposa, utaphunzitsidwa m'cilamulo,
19. nulimbika mumtima kuti iwe wekha uli wotsogolera wa akhungu, nyali ya amene akhala mumdima,