1. Cifukwa cace uli wopanda mau owiringula, munthu iwe, amene uli yense wakuweruza; pakuti m'mene uweruza wina, momwemo udzitsutsa iwe wekha, pakuti iwe wakuweruza, umacita zomwezo.
2. Ndipo tidziwa kuti kuweruza kwa Mulungu kuli koona pa iwo akucita zotere.