1. Cikondi ca pa abale cikhalebe.
2. Musaiwale kucereza alendo; pakuti mwa ici ena anacereza angelo osacidziwa.
3. Kumbukilani am'nsinga, monga am'nsinga anzao; ocitidwa zoipa, monga ngati inunso adatero nanu m'thupi.
4. Ukwati ucitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi acigololo adzawaweruza Mulungu.
5. Mtima wanu ukhale wosakonda cuma; zimene muli nazo zikukwanireni; pakuti iye anati, Sindidzakusiya konse, kungakhale kukutaya, sindidzakutaya ndithu.
6. Kotero kuti tinena molimbika mtima,Mthandizi wanga ndiye Ambuye; smdidzaopa;Adzandicitira ciani munthu?
7. Kumbukilani atsogoleri anu, amene analankhula nanu Mau a Mulungu; ndipo poyang'anira citsiriziro ca mayendedwe ao mutsanze cikhulupiriro cao.
8. Yesu Kristu ali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi ku nthawi zonse.
9. Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundu mitundu, ndi acilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi cisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindula nazo.