16. Ambuye acitire banja la Onesiforo cifundo; pakuti anatsitsimutsa ine kawiri kawiri, ndipo sanacita manyazi ndi unyolo wanga;
17. komatu pokhala m'Roma iye anandifunafuna ine ndi khama, nandipeza,
18. (Ambuye ampatse iye apeze cifundo ndi Ambuye tsiku lijalo); ndi muja ananditumikira m'zinthu zambiri m'Efeso, uzindikira iwe bwino.