7. Pakuti mwamuna sayenera kubvala pamutu, popeza akhala fanizo ndi ulemerero wa Mulungu: koma mkazi ali ulemerero wa mwamuna.
8. Pakuti mwamuna sakhala wa kwa mkazi; koma mkazi wa kwa mwamuna;
9. pakutinso mwamuna sanalengedwa cifukwa ca mkazi;
10. koma mkazi cifukwa ca mwamuna; cifukwa ca ici mkazi ayenera kukhala nao ulamuliro pamutu pace, cifukwa ca angelo.