15. Ndipo Yoswa anacitirana nao mtendere, napangana nao, akhale amoyo; ndi akalonga a msonkhano anawalumbirira,
16. Ndipo kunali, atatha kupangana nao masiku atatu, anamva kuti ndiwo anansi ao, ndi kuti kwao ndi pakati pao,
17. Ndipo ana a Israyeli anayenda ulendo, nafika ku midzi yap tsiku lacitatu. Koma midzi yao ndiyo Gibeoni, ndi Cefira, ndi Beerotu ndi KiriyatuYearimu.
18. Ndipo ana a Israyeli sanawakantha, pakuti akalonga a msonkhano adawalumbirira kwa Yehova, Mulungu wa Israyeli. Ndipo msonkhano wonse unadandaula pa akalonga,