28. Pamenepo ndiopa zisoni zanga zonse,Ndidziwa kuti simudzandiyesa wosacimwa.
29. Mlandu udzanditsutsa;Potero ndigwire nchito cabe cifukwa ninji?
30. Ndikasamba madzi a cipale cofewaNdi kuyeretsa manja anga ndi sopo;
31. Mudzandibviikanso muli zoola,Ndi zobvala zanga zidzanyansidwa nane.
32. Pakuti sindiye munthu, monga ine, kuti ndimyankhe,Kuti tikomane mlandu.