23. Mkwapulo ukapha modzidzimutsa,Adzaseka tsoka la wosacimwa.
24. Dziko lapansi laperekedwa m'dzanja la woipa;Aphimba maso a oweruza ace.Ngati sindiye, pali yaninso?
25. Tsopano masiku anga afulumira kuposa wamtokoma;Athawa osaona cokoma.
26. Apitirira ngati zombo zaliwiro;Ngati mphungu igudukira cakudya cace.
27. Ndikati, Ndidzaiwala condidandaulitsa,Ndidzasintha nkhope yanga yacisoni, ndidzasekerera;