19. Wampatsa kavalo mphamvu yace kodi?Wambveka pakhosi pace cenjerere cogwedezeka?
20. Wamlumphitsa kodi ngati dzombe?Ulemerero wa kumina kwace ngwoopsa.
21. Apalasa kucigwa, nakondwera nayo mphamvu yace;Aturuka kukomana nao eni zida.
22. Aseka mantha osaopsedwa,Osabwerera kuthawa lupanga.