15. Kodi Iye amene anandilenga ine m'mimba sanamlenga iyenso?Sindiye mmodzi anatiumba m'mimba?
16. Ngati ndakaniza aumphawi cifuniro cao,Kapena kutopetsa maso a amasiye,
17. Kapena kudya nthongo yanga ndekha,Osadyako mwana wamasiye;
18. (Pakuti kuyambira ubwana wanga analeredwa ndi ine monga ndi atate;Ndipo ndinakhala nkhoswe ya wamasiye cibadwire ine.)
19. Ngati ndinaona wina alinkutayika wopanda cobvala,Kapena kuti wosowa alibe copfunda;
20. Ngati zuuno zace sizinandiyamika,Ngati sanapfunda ubweya wa nkhosa zanga;
21. Ngati ndinasamulira ana amasiye dzanja langa,Popeza ndinaona thandizo langa kucipata;
22. Libanthuke phewa langa paphalo,Ndi dzanja langa liduke pagwangwa.
23. Pakuti tsoka locokera kwa Mulungu linandiopsa,Ndi cifukwa ca ukulu wace sindinakhoza kanthu,