7. Njira imeneyi palibe ciombankhanga ciidziwa;Lingakhale diso la kabawi losapenyapo.
8. Nyama zodzikuza sizinapondapo,Ngakhale mkango waukali sunapitapo.
9. Munthu atambasulira dzanja lace kumwala;Agubuduza mapiri kuyambira kumizu.
10. Asema njira pakati pa matanthwe,Ndi diso lace liona ciri conse ca mtengo wace.
11. Atseka mitsinje ingadonthe;Naturutsira poyera cobisikaci.
12. Koma nzeru, idzapezeka kuti?Ndi luntha, malo ace ali kuti?
13. Munthu sadziwa mtengo wace;Ndipo silipezeka m'dziko la amoyo.
14. Pozama pakuti, Mwa ine mulibe;Ndi nyanja ikuti, Kwa ine kulibe.
15. Silipezeka ndi golidi,Sayesapo siliva mtengo wace.
16. Sailinganiza ndi golidi wa Ofiri,Ndi sohamu wa mtengo wace wapatali kapena safiro.