19. Apita nao, ansembe atawafunkhica,Nagubuduza amphamvu.
20. Amcotsera wokhulupirika kunena kwace.Nalanda luntha la akulu.
21. Atsanulira mnyozo pa akalonga,Nawasezera olimba lamba lao.
22. Abvumbulutsa zozama mumdima,Naturutsa mthunzi wa imfa ukhale poyera;
23. Acurukitsa amitundu, nawaononganso;Abalalikitsa amitundu, nawabwezanso.
24. Awacotsera akulu a anthu a padziko mtima wao,Nawasokeretsa m'cipululu copanda njira.
25. Iwo ayambasa mumdima mopanda kuunika,Ndipo awayendetsa dzandi dzandi.