6. Ndipo kudzakhala cilimbiko m'nthawi zako, cipulumutso cambiri, nzeru ndi kudziwa; kuopa kwa Yehova ndiko cumacace.
7. Taonani, olimba mtima ao angopfuula kunja, mithenga ya mtendere ilira kowawa.
8. Njira zamakwalala zikufa, kulibe woyendamo; Asuri watyola cipangano, wanyoza midzi, sasamalira anthu.
9. Dziko lilira maliro ndi kulefuka; Lebano ali ndi manyazi, nafota; Saroni afanana ndi cipululu; pa Basana ndi Karimeli papukutika.
10. Tsopano ndidzauka, ati Yehova; tsopano ndidzanyamuka, tsopano ndidzakwezedwa.
11. Inu mudzatenga pakati ndi mungu, mudzabala ziputu; mpweya wanu ndi moto umene udzakumarizani inu.