27. Ndakuyesa iwe nsanja ndi linga mwa anthu anga, kuti udziwe ndi kuyesa njira yao.
28. Onse ali opikisana ndithu, ayendayenda ndi maugogodi; ndiwo mkuwa ndi citsulo; onsewa acita mobvunda;
29. mbvukuto yatenthedwa ndi moto; mthobvu watha ndi moto wa ng'anjo; ayenga cabe; pakuti oipa sacotsedwa.
30. Anthu adzawacha nthale ya siliva, pakuti Yehova wakana iwo.