1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,
2. Uza ana a Israyeli kuti aziturutsa m'cigono akhate onse, ndi onse akukhala nako kukha, ndi onse odetsedwa cifukwa ca akufa;
3. muwaturutse amuna ndi akazi muwaturutsire kunja kwa cigono, kuti angadetse cigono cao, cimene ndikhala m'kati mwacemo.
4. Ndipo ana a Israyeli anacita cotero, nawaturutsira kunja kwa cigono; monga Yehova adanena ndi Mose momwemo ana a Israyeli anacita.
5. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
6. Nena ndi ana a Israyeli, ndi kuti, Mwamuna kapena mkazi akacita cimo liri lonse amacita anthu, kucita mosakhulupirika pa Yehova, nakaparamuladi;