43. Mabanja aose a Asuhamu monga mwa owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu zinai kudza mazana anai.
44. Ana amuna a Aseri monga mwa mabanja ao ndiwo: Yimna, ndiye kholo la banja la Ayimna; Yisivi, ndiye kholo la banja la Ayisivi; Beriya, ndiye kholo la banja la Aberiya.
45. Ana a Beriya ndiwo: Heberi, ndiye kholo la banja la Aheberi; Malikiyeli, ndiye kholo la banja la Amalikiyeli.