1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2. Dzipangire malipenga awiri asiliva; uwasule mapangidwe ace; ucite nao poitana khamu, ndi poyendetsa a m'zigono.
3. Akaliza, khamu lonse lisonkhane kuli iwe ku khomo la cihema cokomanako,
4. Akaliza limodzi, pamenepo akalonga, akuru a zikwi a m'Israyeli, azisonkhana kuli iwe.