8. ana a Parosi zikwi ziwiri mphambu zana limodzi kudza makumi asanu ndi awiri.
9. Ana a Sefatiya, mazana atatu mphambu makumi asanu ndi awiri kudza awiri.
10. Ana a Ara, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza awiri.
11. Ana a Pakati Moabu, a ana a Yesuwa ndi Yoabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi limodzi ndi asanu ndi atatu.
12. Ana a Elamu, cikwi cimodzi mphambu mazana awiri ndi makumi asanu kudza anai.
13. Ana a Zatu, mazana asanu ndi atatu mphambu makumi anai kudza asanu.
14. Ana a Zakai, mazana asanu ndi awiri mphambu makumi asanu ndi limodzi.
15. Ana a Binui, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi anai kudza asanu ndi atatu.
16. Ana a Betai, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
17. Ana a Azigadi, zikwi ziwiri mphambu mazana atatu kudza makumi awiri ndi awiri.
18. Ana a Adonikamu, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu ndi limodzi, kudza asanu ndi awiri.
19. Ana a Bigivai, zikwi ziwiri mphambu makumi asanu ndi limodzi kudza asanu ndi awiri.
20. Ana a Adini, mazana asanu ndi limodzi mphambu makumi asanu kudza asanu.
21. Ana a Aberi, a Hezekiya, makumi asanu ndi anai kudza asanu ndi atatu.
22. Ana a Hasumu, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza asanu ndi atatu.
23. Ana a Bezai, mazana atatu mphambu makumi awiri kudza anai.
24. Ana a Harifi, zana limodzi mphambu khumi ndi awiri.