14. panali mudzi waung'ono muli anthu owerengeka; ndipo inadzako mfumu yaikuru, niizinga ndi nkhondo, nimangapo malinga akuru;
15. koma anapezedwamo mwamuna wanzeru wosauka, yemweyo napulumutsa mudziwo ndi nzeru yace; koma panalibe anthu anakumbukira wosauka ameneyo.
16. Pamenepo ndinati, Nzeru ipambana mphamvu; koma anyoza nzeru ya wosauka, osamvera mau ace.
17. Mau a anzeru acete amveka koposa kupfuula kwa wolamulira mwa zitsiru.
18. Nzeru ipambana zida za nkhondo; koma wocimwa mmodzi aononga zabwino zambiri.